Awa ndi mayeso oyesedwa. Apambaneni kuti mupeze mfundo zopita ku Satifiketi ya Chivomerezo cha Utumiki yanu.
2 Petro 1:3 — Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ________ wake.
ubwino
kufatsa
mʼbado
1 Petro 2:2 — Monga ________ obadwa kumene amalirira mkaka, inunso muzilakalaka mkaka weniweni wauzimu, kuti mukule ndi kukufikitsani ku chipulumutso chanu
zilakolako
makanda
mipando
Hoseya 11:3 — Ndi Ine amene ndinaphunzitsa ________ kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
Efereimu
Asiriya
Samariya
Ahebri 11:6 — Ndipo popanda chikhulupiriro nʼkosatheka kukondweretsa Mulungu, chifukwa aliyense amene amabwera kwa Iye ayenera kukhulupirira kuti Mulungu alipodi ndi kuti Iye amapereka ________ kwa amene akumufunitsitsa.
wosatha
chisomo
mphotho
Machitidwe a Atumwi 3:2 — Ndipo munthu wolumala chibadwire ankanyamulidwa tsiku ndi tsiku kukayikidwa pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola kuti azikapempha amene amalowa ku ________ la Nyumbayo.
chuma
bwalo
mbalame
Machitidwe a Atumwi 3:8 — Iye analumpha ndi kuyamba kuyenda. Kenaka ________ nawo pamodzi mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, akuyenda ndi kulumpha ndiponso kuyamika Mulungu.
waufumu
banja
analowa
Genesis 5:24 — ________ anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
Hamori
Biliha
Enoki
Genesis 6:9 — Mbiri ya Nowa inali yotere: Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a ________ wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu.
Mika 6:8 — Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda ________ ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
Ahebri 12:1 — Tsono popeza ifenso tazunguliridwa ndi gulu lalikulu la mboni, tiyeni titaye chilichonse chimene chimatitchinga, ________ tchimo limene limatikola mosavuta, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu.
makamaka
mwamphamvu
okondedwa
Yesaya 40:31 — koma iwo amene ________ Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.
amakondwera
akulamulira
amakhulupirira
1 Timoteyo 4:8 — Pakuti kulimbitsa ________ kumapindulitsapo pangʼono, koma moyo woopa Mulungu umapindulitsa pa zonse. Umatilonjeza moyo pa moyo uno ndiponso pa moyo umene ukubwerawo.